Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 6:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kunali tsono, atamva Sanibalati, ndi Tobiya, ndi Gesemu M-arabu, ndi adani athu otsala, kuti ndidatha kumanga lingali, posatsalaponso popasuka; (ngakhale pajapo sindinaika zitseko pazipata);

2. anatumiza mau kwa ine Sanibalati ndi Gesemu, kuti, Tiyeni tikomane ku midzi ya ku cigwa ca Ono; koma analingirira za kundicitira coipa.

3. Ndipo ndinawatumizira mithenga, ndi kuti, Ndirikucita nchito yaikuru, sindikhoza kutsika; ndiidulirenji padera nchito poileka ine, ndi kukutsikirani?

4. Nanditumizira ine mau otere kanai; ndinawabwezeranso mau momwemo.

5. Pamenepo Sanibalati anatuma mnyamata wace kwa ine kacisanu, ndi kalata wosatseka m'dzanja mwace;

6. m'menemo mudalembedwa, Kwamveka mwa amitundu, ndi Gasimu acinena, kuti iwe ndi Ayuda mulikulingirira za kupanduka; cifukwa cace mulikumanga lingali; ndipo iwe udzakhala mfumu yao monga mwa mau awa.

7. Ndiponso waika aneneri akubukitsa za iwe ku Yerusalemu, ndi kuti, Ku Yuda kuli mfumu, ndipo zidzamveka kwa mfumu, kuti kuli zotere. Tiyeni tsono tipangane pamodzi.

8. Koma ndinamtumizira mau, akuti, Palibe zinthu zotere zonga unenazi, koma uzilingirira mumtima mwako.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 6