Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 4:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, atamva Sanibalati kuti tinalikumanga lingali, kudamuipira, nakwiya kwakukuru, naseka Ayuda pwepwete.

2. Nanena iye pamaso pa abale ace ndi ankhondo a ku Samariya, nati, Alikucitanji Ayuda ofokawa? adzimangire linga kodi? adzapereka nsembe kodi? adzatsiriza tsiku limodzi kodi? adzakometsanso miyala ya ku miunda yotenthedwa?

3. Ndipo Tobiya M-amoni anali naye, nati, Cinkana ici acimanga, ikakwerako nkhandwe, idzagamula linga lao lamiyala.

4. Imvani, Mulungu wathu, popeza tanyozeka ife; muwabwezere citonzo cao pamtu pao, ndi kuwapereka akhale cofunkhidwa m'dziko la ndende;

5. ndipo musakwirira mphulupulu yao, ndi kulakwa kwao kusafafanizike pamaso panu; pakuti anautsa mkwiyo wanu pamaso pa omanga linga.

6. Koma tinamanga lingali, ndi linga lonse linalumikizana kufikira pakati mpakati; popeza mitima ya anthu inalunjika kunchito.

7. Koma kunali, atamva Sanibalati, ndi Tobiya, ndi Aarabu, ndi Aamoni, ndi Aasidodi, kuti makonzedwe a malinga a Yerusalemu anakula, ndi kuti mopasuka mwace munayamba kutsekeka, cidawaipira kwambiri;

8. napangana ciwembu iwo onse pamodzi, kudzathira nkhondo ku Yerusalemu, ndi kucita cisokonezo m'menemo.

9. Koma tinapemphera kwa Mulungu wathu, ndi kuwaikira olindirira usana ndi usiku, cifukwa ca iwowa.

10. Ndipo Ayuda anati, Mphamvu ya osenza akatundu yatha, ndi dothi licuruka, motero sitidzakhoza kumanga lingali.

11. Nati adani athu, Sadzadziwa kapena kuona mpaka talowa pakati pao, ndi kuwapha, ndi kuleketsa nchitoyi.

12. Ndipo kunali, atafika Ayuda okhala pafupi pao ocokera pamalo ponse, anatiuza ife kakhumi, Bwererani kwa ife.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 4