Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nehemiya 11:20-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndi Aisrayeli otsala, ndiwo ansembe ndi Alevi, anakhala m'midzi yonse ya Yuda, yense m'colowa cace.

21. Koma Anetini anakhala m'Ofeli, ndi Ziya, ndi Gisipa anali oyang'anira Anetini.

22. Ndipo woyang'anira wa Alevi m'Yerusalemu ndiye Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika; mwa ana a Asafu oyimbira ena anayang'anira nchito ya m'nyumba ya Mulungu.

23. Pakuti mfumu inalamulira za iwowa, naikira oyimbira cowathandiza, yense cace pa tsiku lace.

24. Ndi Petatiya mwana wa Mesezabele, wa ana a Zera, mwana wa Yuda, anatumikira mfumu pa mirandu yonse ya anthuwo.

25. Ndi ana ena a Yuda anakhala m'midzi ya ku minda yao, m'Kiriyati Ariba ndi miraga yace, ndi m'Diboni ndi miraga yace, ndi m'Yekabizeeli ndi midzi yace,

26. ndi m'Yesuwa, ndi m'Molada, ndi Betepeleti,

27. ndi m'Hazarisuala, ndi m'Beereseba ndi miraga yace,

28. ndi m'Zikilaga, ndi m'Mekona ndi miraga yace,

29. ndi m'Enirimoni, ndi m'Zora, ndi m'Yarimuti,

30. Zanowa, Adulamu ndi midzi yao, Lakisi ndi minda yace, Azeka ndi miraga yace. Ndipo anamanga misasa kuyambira ku Beereseba mpaka cigwa ca Hinomu.

Werengani mutu wathunthu Nehemiya 11