Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nahumu 2:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma Nineve wakhala ciyambire cace ngati thamanda lamadzi; koma athawa. Imani, Imani! ati, koma palibe woceuka.

9. Funkhani siliva, funkhani golidi; pakuti palibe kutha kwace kwa zosungikazo, kwa cuma ca zipangizo zofunika ziri zonse.

10. Ndiye mopanda kanthu mwacemo ndi mwacabe, ndi wopasuka; ndi mtima usungunuka, ndi maondo aombana, ndi m'zuuno zonse muwawa, ndi nkhope zao zatumbuluka.

11. Iri kuti ngaka ya mikango, ndi podyera misona ya mikango; kumene mkango, waumuna ndi waukazi, ukayenda ndi mwana wa mkango, kopanda wakuiposa?

12. Mkangowo unamwetula zofikira ana ace, nusamira yaikazi yace, nudzaza mapanga ace ndi nyama, ngaka zace ndi zojiwa.

13. Taona, nditsutsana nawe, ati Yehova wa makamu, ndipo ndidzatentha magareta ace m'utsi; ndi lupanga lidzadya misona yako ya mkango; ndipo ndidzacotsa zofunkha zako pa dziko lapansi, ndi mau a mithenga yako sadzamvekanso.

Werengani mutu wathunthu Nahumu 2