Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 9:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti zonsezi ndinazisunga mumtima ndikalondoletu zonsezi; kuti olungama ndi anzeru ndi nchito zao ali m'manja a Mulungu; ngakhale kukonda ngakhale kudana anthu sadziwa; zonse ziri m'tsogolo mwao.

2. Zonse zigwera onse cimodzimodzi; kanthu kamodzi kangogwera wolungama ndi woipa; ngakhale wabwino ndi woyera ndi wodetsedwa: ngakhale wopereka nsembe ndi wosapereka konse; wabwino alingana ndi wocimwa; wolumbira ndi woopa lumbiro.

3. Ici ndi coipa m'zonse zicitidwa pansi pano, cakuti kanthu kamodzi kagwera onse; indetu, mtimanso wa ana a anthu wadzala udio, ndipo misala iri m'mtima wao akali ndi moyo, ndi pamenepo apita kwa akufa.

4. Pakuti woyang'ana ndi amoyo onse ali naco ciyembekezo; pakuti garu wamoyo aposa mkango wakufa.

5. Pakuti amoyo adziwa kuti tidzafa; koma akufa sadziwa kanthu bi, sadzalandira mphotho; pakuti angoiwalika.

6. Cikondi cao ndi mdano wao ndi dumbo lao lomwe zatha tsopano; ndipo nthawi yamuyaya sagawa konse kanthu kali konse kacitidwa pansi pano.

7. Tiye, idya zakudya zako mokondwa, numwe vinyo wako mosekera mtima; pakuti Mulungu wabvomerezeratu zocita zako.

8. Zobvala zako zikhale zoyera masiku onse; mutu wako usasowe mafuta.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 9