Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 9:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti zonsezi ndinazisunga mumtima ndikalondoletu zonsezi; kuti olungama ndi anzeru ndi nchito zao ali m'manja a Mulungu; ngakhale kukonda ngakhale kudana anthu sadziwa; zonse ziri m'tsogolo mwao.

2. Zonse zigwera onse cimodzimodzi; kanthu kamodzi kangogwera wolungama ndi woipa; ngakhale wabwino ndi woyera ndi wodetsedwa: ngakhale wopereka nsembe ndi wosapereka konse; wabwino alingana ndi wocimwa; wolumbira ndi woopa lumbiro.

3. Ici ndi coipa m'zonse zicitidwa pansi pano, cakuti kanthu kamodzi kagwera onse; indetu, mtimanso wa ana a anthu wadzala udio, ndipo misala iri m'mtima wao akali ndi moyo, ndi pamenepo apita kwa akufa.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 9