Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 7:20-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene acita zabwino osacimwa.

21. Mau onsetu onenedwa usawalabadire; kuti usamve kapolo wako alikukutemberera;

22. pakuti kawiri kawiritu mtima wako udziwa kuti nawenso unatemberera ena.

23. Ndayesa zonsezi ndi nzeru; ndinati, Ndidzakhala wanzeru, koma inanditarikira.

24. Cakutari ndi cakuyadi adzacipeza ndani?

25. Ndinapotoka ndi mtima wanga womwe kudziwa ndi kusanthula ndi kufunafuna nzeru ndi malongosoledwe a zinthu, ndi kudziwa kuti udio ndiwo utsiru, ndi kuti kupusa ndi misala;

26. ndipo ndinapeza kanthu kowawa koposa imfa, ndiko mkazi amene ndiye msampha, mtima wace ukunga maukonde, manja ace ndiwo matangadza; yemwe Mulungu amuyesa wabwino adzapulumuka kwa iye; koma wocimwa adzagwidwa naye.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 7