Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 7:15-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndaona zonsezi masiku anga acabe; pali wolungama angofa m'cilungamo cace, ndipo pali woipa angokhalabe ndi moyo m'kuipa kwace.

16. Usapambanitse kukhala wolungama; usakhale wanzeru koposa; bwanji ufuna kudziononga wekha?

17. Usapambanitse kuipa, ngakhale kupusa, uferenji nthawi yako isanafike?

18. Kuli kwabwino kugwira ici; indetu, usacotsepo dzanja lako pakuti yemwe aopa Mulungu adzaturuka monsemo.

19. Nzeru ilimbitsa wanzeru koposa akuru khumi akulamulira m'mudzi.

20. Pakuti kulibe wolungama pansi pano amene acita zabwino osacimwa.

21. Mau onsetu onenedwa usawalabadire; kuti usamve kapolo wako alikukutemberera;

22. pakuti kawiri kawiritu mtima wako udziwa kuti nawenso unatemberera ena.

23. Ndayesa zonsezi ndi nzeru; ndinati, Ndidzakhala wanzeru, koma inanditarikira.

24. Cakutari ndi cakuyadi adzacipeza ndani?

25. Ndinapotoka ndi mtima wanga womwe kudziwa ndi kusanthula ndi kufunafuna nzeru ndi malongosoledwe a zinthu, ndi kudziwa kuti udio ndiwo utsiru, ndi kuti kupusa ndi misala;

26. ndipo ndinapeza kanthu kowawa koposa imfa, ndiko mkazi amene ndiye msampha, mtima wace ukunga maukonde, manja ace ndiwo matangadza; yemwe Mulungu amuyesa wabwino adzapulumuka kwa iye; koma wocimwa adzagwidwa naye.

27. Taonani, ici ndacipeza, ati Mlalikiyo, m'kuphatikiza cinthu cina ndi cinzace, ndikazindikire malongosoledwe ao;

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 7