Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 5:11-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pocuruka katundu, akudyapo acurukanso; nanga apindulira eni ace ciani, koma kungopenyera ndi maso ao?

12. Tulo ta munthu wogwira nchito ntabwino, ngakhale adya pang'ono ngakhale zambiri; koma kukhuta kwa wolemera sikumgonetsa tulo.

13. Pali coipa cobvuta ndaciona kunja kuno, ndico, cuma cirikupweteka eni ace pocikundika;

14. koma cumaco cionongeka pomgwera tsoka; ndipo akabala mwana, m'dzanja lace mulibe kanthu.

15. Monga anaturuka m'mimba ya amace, adzabweranso kupita wamarisece, monga anadza osatenga kanthu pa nchito zace, kakunyamula m'dzanja lace.

16. Icinso ndi coipa cowawa, cakuti adzangopita monse monga anadza; ndipo wodzisautsa cabe adzaona phindu lanji?

17. Inde masiku ace onse amadya mumdima, nizimcurukira cisoni ndi nthenda ndi mkwiyo.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 5