Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 4:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndinabweranso tsono ndi kupenyera nsautso zonse zimacitidwa kunja kuno; ndipo taona, misozi ya otsenderezedwa, koma analibe wakuwatonthoza; ndipo akuwatsendereza anali ndi mphamvu koma iwowa analibe wakuwatonthoza.

2. Ndipo ndinatama akufa atatha kufa kupambana amoyo omwe alipobe;

3. inde yemwe sanabadwe konse aposa onse awiriwo popeza sanaone nchito yoipa yocitidwa kunja kuno.

4. Ndiponso ndinapenyera mabvuto onse ndi nchito zonse zompindulira bwino, kuti cifukwa ca zimenezi anansi ace acitira munthu nsanje. Icinso ndi cabe ndi kungosautsa mtima.

5. Citsiru cimanga manja ace, nicidya nyama yace yace.

6. Dzanja limodzi lodzala pali mtendere liposa manja awiri oti tho pali bvuto ndi kungosautsa mtima.

7. Pamenepo ndinabwera ndi kupenyera zacabe kunja kuno.

8. Pali mmodzi palibe waciwiri; inde, alibe mwana ngakhale mbale; koma nchito yace yonse iribe citsiriziro, ngakhale diso lace silikhuta cuma. Samati, Ndigwira nchito ndi kumana moyo wanga zabwino cifukwa ca yani? Icinso ndi cabe, inde, bvuto lalikuru.

9. Awiri aposa mmodzi; pakuti ali ndi mphotho yabwino m'nchito zao.

10. Pakuti akagwa, wina adzautsa mnzace; koma tsoka wakugwa wopanda womnyamutsa.

11. Ndiponso awiri akagona limodzi afunditsana; koma mmodzi pa yekha kodi adzafunditsidwa bwanji?

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 4