Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 2:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndinadzipangira zazikuru; ndinadzimangira nyumba; ndi kunka mipesa;

5. ndinakonza mphanie ndi minda yanga, ndi kuokamo mitengo ya zipatso za mitundu mitundu;

6. ndinadzipangira ndekha matamanda a madzi akuthirira madzi m'nkhalango momeramo mitengo;

7. ndinadzitengera akapolo ndi adzakazi, ndinali ndi akapolo anabadwa kwanga; ndinalemeranso pokhala nazo zoweta zazikuru ndi zazing'ono kupambana onse anakhala m'Yerusalemu ndisanabadwe ine;

8. ndinakundikanso siliva ndi golidi ndi cuma ca mafumu ndi madera a dziko; ndinaitanitsa amuna ndi akazi akuyimba ndi zokondweretsazo za ana a anthu, ndizo zoyimbira za mitundu mitundu.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 2