Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 2:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndinati mumtima mwanga, Tiyetu, ndikuyese ndi cimwemwe; tapenya tsono zabwino; ndipo taona, icinso ndi cabe.

2. Ndinati, Kuseka ndi misala; ndi cimwemwe kodi cicita ciani?

3. Ndinafuna mumtima mwanga kusangalatsa thupi langa ndi vinyo, mtima wanga ulikunditsogolera mwanzeru, ndi kugwira utsiru, kuti ndizindikire cabwinoco ca ana a anthu nciani cimene azicicita pansi pa thambo masiku onse a moyo wao.

4. Ndinadzipangira zazikuru; ndinadzimangira nyumba; ndi kunka mipesa;

5. ndinakonza mphanie ndi minda yanga, ndi kuokamo mitengo ya zipatso za mitundu mitundu;

6. ndinadzipangira ndekha matamanda a madzi akuthirira madzi m'nkhalango momeramo mitengo;

7. ndinadzitengera akapolo ndi adzakazi, ndinali ndi akapolo anabadwa kwanga; ndinalemeranso pokhala nazo zoweta zazikuru ndi zazing'ono kupambana onse anakhala m'Yerusalemu ndisanabadwe ine;

8. ndinakundikanso siliva ndi golidi ndi cuma ca mafumu ndi madera a dziko; ndinaitanitsa amuna ndi akazi akuyimba ndi zokondweretsazo za ana a anthu, ndizo zoyimbira za mitundu mitundu.

9. Ndinakula cikulire kupambana onse anali m'Yerusalemu ndisanabadwe ine; ndipo nzeru yanganso inakhala nanebe.

10. Ndipo ciri conse maso anga anacifuna sindinawamana; sindinakaniza mtima wanga cimwemwe ciri conse pakuti mtima wanga unakondwera ndi nchito zanga zonse; gawo langa la m'nchito zanga zonse ndi limeneli.

11. Pamenepo ndinayang'ana zonse manja anga anazipanga, ndi nchito zonse ndinasauka pozigwira; ndipo taona, zonse zinali zacabecabe ndi kungosautsa mtima, ndipo kunalibe phindu kunja kuno.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 2