1. MAU a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya m'Yerusalemu.
2. Zacabecabe, ati Mlaliki; zacabecabe zonse ndi cabe.
3. Kodi nchito zace zonse munthu asauka nazo zimpindulira ciani?
4. Mbadwo wina opita, mbadwo wina nufika; koma dziko lingokhalabe masiku onse,
5. inde dzuwa lituruka, nililowa, nilifulumira komwe linaturukako.
6. Kulowa kumwela ndi kuzungulira: kumpoto zungulire zungulire imaomba mphepo; ibweranso monga mwa mazunguliridwe ace.