Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mlaliki 1:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MAU a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya m'Yerusalemu.

2. Zacabecabe, ati Mlaliki; zacabecabe zonse ndi cabe.

3. Kodi nchito zace zonse munthu asauka nazo zimpindulira ciani?

4. Mbadwo wina opita, mbadwo wina nufika; koma dziko lingokhalabe masiku onse,

5. inde dzuwa lituruka, nililowa, nilifulumira komwe linaturukako.

6. Kulowa kumwela ndi kuzungulira: kumpoto zungulire zungulire imaomba mphepo; ibweranso monga mwa mazunguliridwe ace.

Werengani mutu wathunthu Mlaliki 1