9. Lemekeza Yehova ndi cuma cako,Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;
10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.
11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;
12. Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.
13. Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;
14. Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,Phindu lace liposa golidi woyengeka.
15. Mtengo wace uposa ngale;Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.
16. Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lace;Cuma ndi ulemu m'dzanja lace lamanzere.
17. Njira zace ziri zokondweretsa,Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.
18. Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;Wakulumirira ngwodala.
19. Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;Naika zamwamba ndi luntha.
20. Zakuya zinang'ambika ndi kudziwakwace;Thambo ligwetsa mame.
21. Mwananga, zisacokere ku maso ako;Sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;
22. Ndipo mtima wako udzatengapo moyo,Ndi khosi lako cisomo.
23. Pompo udzayenda m'njira yako osaopa,Osapunthwa phazi lako.
24. Ukagona, sudzacita mantha;Udzagona tulo tokondweretsa.
25. Usaope zoopsya zodzidzimutsa,Ngakhale zikadza zopasula oipa;
26. Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,Nadzasunga phazi lako lingakodwe.