Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 3:9-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Lemekeza Yehova ndi cuma cako,Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;

10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;

12. Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.

13. Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;

14. Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,Phindu lace liposa golidi woyengeka.

15. Mtengo wace uposa ngale;Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

16. Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lace;Cuma ndi ulemu m'dzanja lace lamanzere.

17. Njira zace ziri zokondweretsa,Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.

18. Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;Wakulumirira ngwodala.

19. Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;Naika zamwamba ndi luntha.

20. Zakuya zinang'ambika ndi kudziwakwace;Thambo ligwetsa mame.

21. Mwananga, zisacokere ku maso ako;Sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

22. Ndipo mtima wako udzatengapo moyo,Ndi khosi lako cisomo.

23. Pompo udzayenda m'njira yako osaopa,Osapunthwa phazi lako.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 3