8. Mitsempha yako idzalandirapo moyo,Ndi mafupa ako uwisi.
9. Lemekeza Yehova ndi cuma cako,Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;
10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.
11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;
12. Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.
13. Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;