Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 3:3-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Cifundo ndi coonadi zisakusiye;Uzimange pakhosi pako;Uzilembe pamtima pako;

4. Motero udzapezakisomo ndi nzeru yabwino,Pamaso pa Mulungu ndi anthu.

5. Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,Osacirikizika pa luntha lako;

6. Umlemekeze m'njira zako zonse,Ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

7. Usadziyese wekha wanzeru;Opa Yehova, nupatuke pazoipa;

8. Mitsempha yako idzalandirapo moyo,Ndi mafupa ako uwisi.

9. Lemekeza Yehova ndi cuma cako,Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;

10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;

12. Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.

13. Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;

14. Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,Phindu lace liposa golidi woyengeka.

15. Mtengo wace uposa ngale;Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

16. Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lace;Cuma ndi ulemu m'dzanja lace lamanzere.

17. Njira zace ziri zokondweretsa,Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 3