Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 3:26-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,Nadzasunga phazi lako lingakodwe.

27. Oyenera kulandira zabwino usawamane;Pokhoza dzanja lako kuwacitira zabwino.

28. Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,Ndipo mawa ndidzakupatsa;Pokhala uli nako kanthu.

29. Usapangire mnzako ciwembu;Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.

30. Usakangane ndi munthu cabe,Ngati sanakucitira coipa,

31. Usacitire nsanje munthu waciwawa;Usasankhe njira yace iri yonse.

32. Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;Koma cinsinsi cace ciri ndi oongoka.

33. Mulungu atemberera za m'nyumba ya woipa;Koma adalitsa mokhalamo olungama.

34. Anyozadi akunyoza,Koma apatsa akufatsa cisomo.

35. Anzeru adzalandira ulemu colowa cao;Koma opusa adzakweza manyazi.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 3