22. Ndipo mtima wako udzatengapo moyo,Ndi khosi lako cisomo.
23. Pompo udzayenda m'njira yako osaopa,Osapunthwa phazi lako.
24. Ukagona, sudzacita mantha;Udzagona tulo tokondweretsa.
25. Usaope zoopsya zodzidzimutsa,Ngakhale zikadza zopasula oipa;
26. Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,Nadzasunga phazi lako lingakodwe.
27. Oyenera kulandira zabwino usawamane;Pokhoza dzanja lako kuwacitira zabwino.
28. Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,Ndipo mawa ndidzakupatsa;Pokhala uli nako kanthu.
29. Usapangire mnzako ciwembu;Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.
30. Usakangane ndi munthu cabe,Ngati sanakucitira coipa,