Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 3:20-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Zakuya zinang'ambika ndi kudziwakwace;Thambo ligwetsa mame.

21. Mwananga, zisacokere ku maso ako;Sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

22. Ndipo mtima wako udzatengapo moyo,Ndi khosi lako cisomo.

23. Pompo udzayenda m'njira yako osaopa,Osapunthwa phazi lako.

24. Ukagona, sudzacita mantha;Udzagona tulo tokondweretsa.

25. Usaope zoopsya zodzidzimutsa,Ngakhale zikadza zopasula oipa;

26. Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako,Nadzasunga phazi lako lingakodwe.

27. Oyenera kulandira zabwino usawamane;Pokhoza dzanja lako kuwacitira zabwino.

28. Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso,Ndipo mawa ndidzakupatsa;Pokhala uli nako kanthu.

29. Usapangire mnzako ciwembu;Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.

30. Usakangane ndi munthu cabe,Ngati sanakucitira coipa,

31. Usacitire nsanje munthu waciwawa;Usasankhe njira yace iri yonse.

32. Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova;Koma cinsinsi cace ciri ndi oongoka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 3