1. Mwananga, usaiwale malamulo anga,Mtima wako usunge malangizo anga;
2. Pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,Ndi zaka za moyo ndi mtendere.
3. Cifundo ndi coonadi zisakusiye;Uzimange pakhosi pako;Uzilembe pamtima pako;
4. Motero udzapezakisomo ndi nzeru yabwino,Pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5. Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,Osacirikizika pa luntha lako;
6. Umlemekeze m'njira zako zonse,Ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.
7. Usadziyese wekha wanzeru;Opa Yehova, nupatuke pazoipa;
8. Mitsempha yako idzalandirapo moyo,Ndi mafupa ako uwisi.
9. Lemekeza Yehova ndi cuma cako,Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;
10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.
11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;
12. Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.
13. Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;