Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 3:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwananga, usaiwale malamulo anga,Mtima wako usunge malangizo anga;

2. Pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,Ndi zaka za moyo ndi mtendere.

3. Cifundo ndi coonadi zisakusiye;Uzimange pakhosi pako;Uzilembe pamtima pako;

4. Motero udzapezakisomo ndi nzeru yabwino,Pamaso pa Mulungu ndi anthu.

5. Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,Osacirikizika pa luntha lako;

6. Umlemekeze m'njira zako zonse,Ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

7. Usadziyese wekha wanzeru;Opa Yehova, nupatuke pazoipa;

8. Mitsempha yako idzalandirapo moyo,Ndi mafupa ako uwisi.

9. Lemekeza Yehova ndi cuma cako,Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;

10. Motero nkhokwe zako zidzangoti the,Mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11. Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 3