Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 27:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mwala ulemera, mcenga ndiwo katundu;Koma mkwiyo wa citsiru upambana kulemera kwace.

4. Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka;Koma ndani angalakike ndi nsanje?

5. Cidzudzulo comveka ciposa cikondi cobisika.

6. Kulasa kwa bwenzi kulikokhulupirika;Koma mdani apsompsona kawiri kawiri.

7. Mtima wokhuta upondereza cisa ca uci;Koma wakumva njala ayesa zowawa zonse zotsekemera.

8. Monga mbalame yosocera ku cisa cace,Momwemo munthu wosocera ku malo ace.

9. Mafuta ndi zonunkhira zikondweretsa mtima,Ndi ubwino wa bwenzi uteronso pakupangira uphungu,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 27