Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 24:8-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Wolingalira zakucita zoipaAnthu adzamcha waciwembu.

9. Maganizo opusa ndiwo cimo;Wonyoza anyansa anthu.

10. Ukalefuka tsiku la tsokaMphamvu yako icepa.

11. Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse;Omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.

12. Ukanena, Taonani, sitinadziwa cimeneci;Kodi woyesa mitima sacizindikira ici?Ndi wosunga moyo wako kodi sacidziwa?Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa macitidwe ace?

13. Mwananga, idya uci pakuti ngwabwino,Ndi cisa cace citsekemera m'kamwamwako;

14. Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

15. Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.

16. Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.

17. Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;

18. Kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa,Ndi kuleka kumkwiyira.

19. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa;Ngakhale kucitira nsanje amphulupulu;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 24