Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 24:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo,Ndi kupulumuka pocuruka aphungu,

7. Nzeru itarikira citsiru;Satsegula pakamwa kubwalo.

8. Wolingalira zakucita zoipaAnthu adzamcha waciwembu.

9. Maganizo opusa ndiwo cimo;Wonyoza anyansa anthu.

10. Ukalefuka tsiku la tsokaMphamvu yako icepa.

11. Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse;Omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.

12. Ukanena, Taonani, sitinadziwa cimeneci;Kodi woyesa mitima sacizindikira ici?Ndi wosunga moyo wako kodi sacidziwa?Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa macitidwe ace?

Werengani mutu wathunthu Miyambi 24