13. Mwananga, idya uci pakuti ngwabwino,Ndi cisa cace citsekemera m'kamwamwako;
14. Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.
15. Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.
16. Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.
17. Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;