Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 24:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Mwananga, idya uci pakuti ngwabwino,Ndi cisa cace citsekemera m'kamwamwako;

14. Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

15. Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.

16. Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.

17. Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 24