Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 24:1-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Usacitire nsanje anthu oipa, Ngakhale kufuna kukhala nao;

2. Pakuti mtima wao ulingalira za cionongeko;Milomo yao ilankhula za mphulupulu.

3. Nzeru imangitsa nyumba;Luntha liikhazikitsa.

4. Kudziwa kudzaza zipinda zaceNdi cuma conse cofunika ca mtengo wace.

5. Mwamuna wanzeru ngwamphamvu;Munthu wodziwa ankabe nalimba.

6. Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo,Ndi kupulumuka pocuruka aphungu,

7. Nzeru itarikira citsiru;Satsegula pakamwa kubwalo.

8. Wolingalira zakucita zoipaAnthu adzamcha waciwembu.

9. Maganizo opusa ndiwo cimo;Wonyoza anyansa anthu.

10. Ukalefuka tsiku la tsokaMphamvu yako icepa.

11. Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse;Omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.

12. Ukanena, Taonani, sitinadziwa cimeneci;Kodi woyesa mitima sacizindikira ici?Ndi wosunga moyo wako kodi sacidziwa?Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa macitidwe ace?

13. Mwananga, idya uci pakuti ngwabwino,Ndi cisa cace citsekemera m'kamwamwako;

14. Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

15. Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 24