1. Usacitire nsanje anthu oipa, Ngakhale kufuna kukhala nao;
2. Pakuti mtima wao ulingalira za cionongeko;Milomo yao ilankhula za mphulupulu.
3. Nzeru imangitsa nyumba;Luntha liikhazikitsa.
4. Kudziwa kudzaza zipinda zaceNdi cuma conse cofunika ca mtengo wace.
5. Mwamuna wanzeru ngwamphamvu;Munthu wodziwa ankabe nalimba.
6. Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo,Ndi kupulumuka pocuruka aphungu,
7. Nzeru itarikira citsiru;Satsegula pakamwa kubwalo.
8. Wolingalira zakucita zoipaAnthu adzamcha waciwembu.
9. Maganizo opusa ndiwo cimo;Wonyoza anyansa anthu.
10. Ukalefuka tsiku la tsokaMphamvu yako icepa.
11. Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse;Omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.
12. Ukanena, Taonani, sitinadziwa cimeneci;Kodi woyesa mitima sacizindikira ici?Ndi wosunga moyo wako kodi sacidziwa?Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa macitidwe ace?