9. Pamenepo udzazindikira cilungamo ndi ciweruzo,Zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.
10. Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako,Moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,
11. Kulingalira kudzakudikira,Kuzindikira kudzakucinjiriza;
12. Kukupulumutsa ku njira yoipa,Kwa anthu onena zokhota;
13. Akusiya mayendedwe olungama,Akayende m'njira za mdima;
14. Omwe asangalala pocita zoipa,Nakondwera ndi zokhota zoipa;