Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 2:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pamenepo udzazindikira cilungamo ndi ciweruzo,Zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10. Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako,Moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

11. Kulingalira kudzakudikira,Kuzindikira kudzakucinjiriza;

12. Kukupulumutsa ku njira yoipa,Kwa anthu onena zokhota;

13. Akusiya mayendedwe olungama,Akayende m'njira za mdima;

14. Omwe asangalala pocita zoipa,Nakondwera ndi zokhota zoipa;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 2