Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 2:3-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ukaitananso luntha,Ndi kupfuulira kuti ukazindikire;

4. Ukaifunafuna ngati siliva,Ndi kuipwaira ngati cuma cobisika;

5. Pompo udzazindikira kuopa YehovaNdi kumdziwadi Mulungu.

6. Pakuti Yehova apatsa nzeru;Kudziwa ndi kuzindikira kuturuka m'kamwa mwace;

7. Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni;Ndiye cikopa ca oyenda molunjika;

8. Kuti acinjirize njira za ciweruzo,Nadikire khwalala la opatulidwa ace.

9. Pamenepo udzazindikira cilungamo ndi ciweruzo,Zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10. Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako,Moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

11. Kulingalira kudzakudikira,Kuzindikira kudzakucinjiriza;

12. Kukupulumutsa ku njira yoipa,Kwa anthu onena zokhota;

13. Akusiya mayendedwe olungama,Akayende m'njira za mdima;

14. Omwe asangalala pocita zoipa,Nakondwera ndi zokhota zoipa;

15. Amene apotoza njira zao,Nakhotetsa mayendedwe ao;

16. Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi waciwerewere,Kwa mkazi wacilendo wosyasyalika ndi mau ace;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 2