2. Kucherera makutu ako kunzeru,Kulozetsa mtima wako kukuzindikira;
3. Ukaitananso luntha,Ndi kupfuulira kuti ukazindikire;
4. Ukaifunafuna ngati siliva,Ndi kuipwaira ngati cuma cobisika;
5. Pompo udzazindikira kuopa YehovaNdi kumdziwadi Mulungu.
6. Pakuti Yehova apatsa nzeru;Kudziwa ndi kuzindikira kuturuka m'kamwa mwace;
7. Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni;Ndiye cikopa ca oyenda molunjika;
8. Kuti acinjirize njira za ciweruzo,Nadikire khwalala la opatulidwa ace.
9. Pamenepo udzazindikira cilungamo ndi ciweruzo,Zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.