Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 2:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Amene apotoza njira zao,Nakhotetsa mayendedwe ao;

16. Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi waciwerewere,Kwa mkazi wacilendo wosyasyalika ndi mau ace;

17. Wosiya bwenzi la ubwana wace,Naiwala cipangano ca Mulungu wace;

18. Nyumba yace itsikira kuimfa,Ndi mayendedwe ace kwa akufa;

19. Onse akunka kwa iye sabweranso,Safika ku njira za moyo;

20. Nzeru idzakuyendetsa m'njira ya anthu abwino,Kuti usunge mayendedwe a olungama.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 2