Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 2:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwananga, ukalandira mau anga,Ndi kusunga malamulo anga;

2. Kucherera makutu ako kunzeru,Kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

3. Ukaitananso luntha,Ndi kupfuulira kuti ukazindikire;

4. Ukaifunafuna ngati siliva,Ndi kuipwaira ngati cuma cobisika;

5. Pompo udzazindikira kuopa YehovaNdi kumdziwadi Mulungu.

6. Pakuti Yehova apatsa nzeru;Kudziwa ndi kuzindikira kuturuka m'kamwa mwace;

7. Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni;Ndiye cikopa ca oyenda molunjika;

8. Kuti acinjirize njira za ciweruzo,Nadikire khwalala la opatulidwa ace.

9. Pamenepo udzazindikira cilungamo ndi ciweruzo,Zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10. Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako,Moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 2