Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 18:8-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,Zotsikira m'kati mwa mimba.

9. Wogwira nchito mwaulesiNdiye mbale wace wa wosakaza.

10. Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;Wolungama athamangiramo napulumuka.

11. Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;Alingalira kuti ndico khoma lalitari.

12. Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;Koma cifatso citsogolera ulemu.

13. Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.

14. Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?

15. Mtima wa wozindikira umaphunzira;Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

16. Mtulo wa munthu umtsegulira njira,Numfikitsa pamaso pa akuru.

17. Woyamba kudzinenera ayang'anika wolungama;Koma mnzace afika namuululitsa zace zonse.

18. Ula uletsa makangano,Nulekanitsa amphamvu.

19. Kupembedza mbale utamcimwira nkobvuta,Kulanda mudzi wolimba nkosabvuta;Makangano akunga mipiringidzo ya linga.

20. Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m'kamwa mwace;Iye nadzakhuta phindu la milomo yace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 18