Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 18:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. M'kamwa mwa wopusa mumuononga,Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.

8. Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,Zotsikira m'kati mwa mimba.

9. Wogwira nchito mwaulesiNdiye mbale wace wa wosakaza.

10. Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;Wolungama athamangiramo napulumuka.

11. Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;Alingalira kuti ndico khoma lalitari.

12. Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;Koma cifatso citsogolera ulemu.

13. Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.

14. Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?

15. Mtima wa wozindikira umaphunzira;Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 18