7. M'kamwa mwa wopusa mumuononga,Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.
8. Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,Zotsikira m'kati mwa mimba.
9. Wogwira nchito mwaulesiNdiye mbale wace wa wosakaza.
10. Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;Wolungama athamangiramo napulumuka.
11. Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;Alingalira kuti ndico khoma lalitari.
12. Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;Koma cifatso citsogolera ulemu.
13. Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.
14. Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?
15. Mtima wa wozindikira umaphunzira;Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.