Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 18:5-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankhu sikuli kwabwino,Ngakhale kucitira cetera wolungama.

6. Milomo ya wopusa ifikitsa makangano;Ndipo m'kamwa mwace muputa kukwapulidwa.

7. M'kamwa mwa wopusa mumuononga,Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.

8. Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,Zotsikira m'kati mwa mimba.

9. Wogwira nchito mwaulesiNdiye mbale wace wa wosakaza.

10. Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;Wolungama athamangiramo napulumuka.

11. Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;Alingalira kuti ndico khoma lalitari.

12. Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;Koma cifatso citsogolera ulemu.

13. Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.

14. Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?

Werengani mutu wathunthu Miyambi 18