Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 18:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Kupembedza mbale utamcimwira nkobvuta,Kulanda mudzi wolimba nkosabvuta;Makangano akunga mipiringidzo ya linga.

20. Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m'kamwa mwace;Iye nadzakhuta phindu la milomo yace.

21. Lilime liri ndi mphamvu pa imfa ndi moyo;Wolikonda adzadya zipatso zace.

22. Wopeza mkazi apeza cinthu cabwino;Yehova amkomera mtima.

23. Wosauka amadandaulira;Koma wolemera ayankha mwaukali.

24. Woyanjana ndi ambiri angodziononga;Koma liripo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 18