11. Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba;Alingalira kuti ndico khoma lalitari.
12. Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;Koma cifatso citsogolera ulemu.
13. Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.
14. Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?
15. Mtima wa wozindikira umaphunzira;Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.
16. Mtulo wa munthu umtsegulira njira,Numfikitsa pamaso pa akuru.