Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 18:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wopanduka afunafuna niro cace,Nakangana ndi nzeru yonse yeniyeni.

2. Wopusa sakondwera ndi kuzindikira;Koma kungobvumbulutsa za m'mtima mwace.

3. Pakudza wamphulupulu padzanso kunyoza;Manyazi natsagana ndi citonzo.

4. Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya;Kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.

5. Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankhu sikuli kwabwino,Ngakhale kucitira cetera wolungama.

6. Milomo ya wopusa ifikitsa makangano;Ndipo m'kamwa mwace muputa kukwapulidwa.

7. M'kamwa mwa wopusa mumuononga,Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.

8. Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka,Zotsikira m'kati mwa mimba.

9. Wogwira nchito mwaulesiNdiye mbale wace wa wosakaza.

10. Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;Wolungama athamangiramo napulumuka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 18