Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 15:8-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Nsembe ya oipa inyansa Yehova;Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.

9. Njira ya oipa inyansa Yehova;Koma akonda wolondola cilungamo.

10. Wosiya njira adzalangidwa mowawa;Wakuda cidzudzulo adzafa.

11. Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?

12. Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,Samapita kwa anzeru.

13. Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.

14. Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

15. Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.

16. Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,

17. Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

18. Munthu wozaza aputa makani;Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

19. Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.

20. Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.

21. Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.

22. Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.

23. Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?

Werengani mutu wathunthu Miyambi 15