7. Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru,Koma mtima wa opusa suli wolungama.
8. Nsembe ya oipa inyansa Yehova;Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.
9. Njira ya oipa inyansa Yehova;Koma akonda wolondola cilungamo.
10. Wosiya njira adzalangidwa mowawa;Wakuda cidzudzulo adzafa.
11. Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?
12. Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,Samapita kwa anzeru.
13. Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.
14. Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.
15. Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.
16. Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,
17. Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.