Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 15:4-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Kuciza lilime ndiko mtengo wa moyo;Koma likakhota liswa moyo.

5. Citsiru cipeputsa mwambo wa atate wace;Koma wosamalira cidzudzulo amacenjera.

6. M'nyumba ya wolungama muli katundu wambiri;Koma m'phindu la woipa muli bvuto,

7. Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru,Koma mtima wa opusa suli wolungama.

8. Nsembe ya oipa inyansa Yehova;Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.

9. Njira ya oipa inyansa Yehova;Koma akonda wolondola cilungamo.

10. Wosiya njira adzalangidwa mowawa;Wakuda cidzudzulo adzafa.

11. Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?

12. Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,Samapita kwa anzeru.

13. Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.

14. Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

15. Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.

16. Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,

17. Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

18. Munthu wozaza aputa makani;Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

19. Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.

20. Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 15