Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 15:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,

26. Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.

27. Wopindula monyenga abvuta nyumba yace;Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.

28. Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.

29. Yehova atarikira oipa;Koma pemphero la olungama alimvera.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 15