Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 15:20-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.

21. Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.

22. Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.

23. Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?

24. Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.

25. Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,

26. Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 15