14. Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.
15. Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.
16. Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,
17. Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.
18. Munthu wozaza aputa makani;Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.
19. Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.
20. Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.
21. Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.
22. Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.
23. Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?
24. Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.
25. Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,
26. Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.
27. Wopindula monyenga abvuta nyumba yace;Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.
28. Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.
29. Yehova atarikira oipa;Koma pemphero la olungama alimvera.