Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 15:11-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?

12. Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,Samapita kwa anzeru.

13. Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.

14. Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

15. Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.

16. Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,

17. Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

18. Munthu wozaza aputa makani;Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

19. Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.

20. Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.

21. Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.

22. Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.

23. Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?

24. Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.

25. Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,

26. Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.

27. Wopindula monyenga abvuta nyumba yace;Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.

28. Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.

29. Yehova atarikira oipa;Koma pemphero la olungama alimvera.

30. Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima;Ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 15