10. Wosiya njira adzalangidwa mowawa;Wakuda cidzudzulo adzafa.
11. Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?
12. Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,Samapita kwa anzeru.
13. Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.
14. Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.
15. Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.