1. Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo;Koma mau owawitsa aputa msunamo.
2. Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.
3. Maso a Yehova ali ponseponse,Nayang'anira oipa ndi abwino.
4. Kuciza lilime ndiko mtengo wa moyo;Koma likakhota liswa moyo.
5. Citsiru cipeputsa mwambo wa atate wace;Koma wosamalira cidzudzulo amacenjera.
6. M'nyumba ya wolungama muli katundu wambiri;Koma m'phindu la woipa muli bvuto,