Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 15:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo;Koma mau owawitsa aputa msunamo.

2. Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.

3. Maso a Yehova ali ponseponse,Nayang'anira oipa ndi abwino.

4. Kuciza lilime ndiko mtengo wa moyo;Koma likakhota liswa moyo.

5. Citsiru cipeputsa mwambo wa atate wace;Koma wosamalira cidzudzulo amacenjera.

6. M'nyumba ya wolungama muli katundu wambiri;Koma m'phindu la woipa muli bvuto,

7. Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru,Koma mtima wa opusa suli wolungama.

8. Nsembe ya oipa inyansa Yehova;Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.

9. Njira ya oipa inyansa Yehova;Koma akonda wolondola cilungamo.

10. Wosiya njira adzalangidwa mowawa;Wakuda cidzudzulo adzafa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 15