Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 14:9-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Zitsiru zinyoza kuparamula;Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.

10. Mtima udziwa kuwawa kwace kwace;Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.

11. Nyumba ya oipa idzapasuka;Koma hema wa oongoka mtima adzakula.

12. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

13. Ngakhale m'kuseka mtima uwawa;Ndipo matsiriziro a ciphwete ndi cisoni.

14. Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira zace;Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.

15. Wacibwana akhulupirira mau onse;Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.

16. Wanzeru amaopa nasiya zoipa;Koma wopusa amanyada osatekeseka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 14